Masalmo 22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Posautsidwa Davide adandaulira, apemphera, ayamika Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo; pa Ajelet Hasakara, Salmo la Davide.

1. Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?Mukhaliranji kutali kwa cipulumutso canga, ndi kwa mau a kubuula kwanga?

2. Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simubvomereza;Ndipo usiku, sindikhala cete.

3. Koma Inu ndinu woyera,Wakukhala m'malemekezo a Israyeli.

4. Makolo athu anakhulupirira Inu:Anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.

5. Anapfuula kwa Inu, napulumutsidwa:Anakhulupita Inu, ndipo sanacita manyazi.

6. Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai:Cotonza ca anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.

7. Onse akundipenya andiseka:Akwenzula, apukusa mutu, nati,

8. Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,Amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

9. Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa:Wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.

10. Cibadwire ine anandisiyira Inu:Kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.

11. Musandikhalire kutali; pakuti nsautso iri pafupi:Pakuti palibe mthandizi.

12. Ng'ombe zamphongo zambiri zandizinga:Mphongo zolimba za ku Basana zandizungulira,

13. Andiyasamira m'kamwa mwao,Ngati mkango wozomola ndi wobangula.

14. Ndathiridwa pansi monga madzi,Ndipo mafupa anga onse anaguluka:Mtima wanga ukunga sera; Wasungunuka m'kati mwa matumbo anga,

15. Mphamvu yanga yauma ngati phale;Ndi lilime langa likangamira ku nsaya zanga;Ndipo mwandifikitsa ku pfumbi la imfa.

16. Pakuti andizinga agaru:Msonkhano wa oipa wanditsekereza;Andiboola m'manja anga ndi m'mapazi anga.

17. Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;Iwo ayang'ana nandipenyetsetsa ine:

18. Agawana zobvala zanga,Nalota maere pa malaya anga,

19. Koma Inu, Yehova, musakhale kutari;Mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

20. Landitsani moyo wanga kulupanga;Wokondedwa wanga ku mphamvu ya garu,

21. Ndipulumutseni m'kamwa mwa mkango;Inde mwandiyankha ine ndiri pa nyanga za njati,

22. Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga:Pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.

23. Inu akuopa Yehova, mumlemekeze;Inu nonse mbumba ya Yakobo, mumcitire ulemu;Ndipo mucite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israyeli.

24. Pakuti sanapeputsa ndipo sananyansidwa ndi zunzo la wozunzika;Ndipo sanambisira nkhope yace;Koma pompfuulira Iye, anamva.

25. Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukuru:Zowinda zanga ndidzazicita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

26. Ozunzika adzadya nadzakhuta:Adzayamika Yehova iwo amene amfuna:Ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.

27. Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukila nadzatembenukira kwa Yehova:Ndipo mafuko onse a amitundu adzagwadira pamaso panu.

28. Pakuti ufumuwo ngwa Yehova;Iye acita ufumu mwa amitundu.

29. Onenepa onse a pa dziko lapansi adzadya nadzagwadira:Onse akutsikira kupfumbi adzawerama pamaso pace,Ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wace.

30. Mbumba ya anthu idzamtumikira;Kudzanenedwa za Ambuye ku mibadwo yakudza.

31. Iwo adzadza nadzafotokozera cilungamo caceKwa anthu akadzabadwa, kuti Iye anacicita.