Masalmo 82 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Oweruza aweruze bwino

Salmo la Asatu.

1. Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu,Aweruza pakati pa milungu.

2. Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,Ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3. Weruzani osauka ndi amasiye;Weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4. Pulumutsani osauka ndi aumphawi:Alanditseni m'dzanja la oipa,

5. Sadziwa, ndipo sazindikira;Amayendayenda mumdima;Maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6. Ndinati Ine, Inu ndinu milungu,Ndi ana a Wam'mwambamwamba nonsenu.

7. Komatu mudzafa monga anthu,Ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.

8. Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi;Pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.