Masalmo 37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Kusangalala kwa ocimwa kudzatha, olungama akhalitsa nathandizidwa ndi Mulungu

Salmo la Davide.

1. Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa,Usacite nsanje cifukwa ca ocita cosalungama.

2. Pakuti adzawamweta msanga monga udzu,Ndipo adzafota monga msipu wauwisi.

3. Khulupirira Yehova, ndipo cita cokoma;Khala m'dziko, ndipo tsata coonadi.

4. Udzikondweretsenso mwa Yehova;Ndipo iye adzakupatsa zokhumba mtima wako.

5. Pereka njira yako kwa Yehova; Khulupiriranso Iye, adzacicita.

6. Ndipo adzaonetsa cilungamo cako monga kuunika,Ndi kuweruza kwako monga usana.

7. Khala cete mwa Yehova, numlindirire Iye:Usabvutike mtima cifukwa ca iye wolemerera m'njira yace,Cifukwa ca munthu wakucita ciwembu.

8. Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo:Usabvutike mtima ungacite coipa,

9. Pakuti ocita zoipa adzadulidwa:Koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi.

10. Katsala kanthawi ndipo woipa adzatha psiti:Inde, udzayang'anira mbuto yace, nudzapeza palibe.

11. Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi;Nadzakondwera nao mtendere wocuruka.

12. Woipa apangira ciwembu wolungama,Namkukutira mano.

13. Ambuye adzamseka:Popeza apenya kuti tsiku lace likudza.

14. Oipa anasolola lupanga, nakoka uta wao;Alikhe ozunzika ndi aumphawi,Aphe amene ali oongoka m'njira:

15. Lupanga lao lidzalowa m'mtima mwao momwe,Ndipo mauta ao adzatyoledwa.

16. Zocepa zace za wolungama zikomaKoposa kucuruka kwao kwa oipa ambiri.

17. Pakuti manja a oipa adzatyoledwa:Koma Yehova acirikiza olungama.

18. Yehova adziwa masiku a anthu angwiro:Ndipo cosiyira cao cidzakhala cosatha.

19. Sadzacita manyazi m'nyengo yoipa:Ndipo m'masiku a njala adzakhuta.

20. Pakuti oipa adzatayika,Ndipo adani ace a Yehova adzanga mafuta a ana a nkhosa:Adzanyeka, monga utsi adzakanganuka.

21. Woipa akongola, wosabweza:Koma wolungama acitira cifundo, napereka.

22. Pakuti iwo amene awadalitsa adzalandira dziko lapansi;Koma iwo amene awatemberera adzadulidwa.

23. Yehova akhazikitsa mayendedwe a munthu;Ndipo akondwera nayo njira yace.

24. Angakhale akagwa, satayikiratu:Pakuti Yehova agwira dzanja lace.

25. Ndinali mwana ndipo ndakalamba:Ndipo sindinapenya wolungama wasiyidwa,Kapena mbumba zace zirinkupempha cakudya.

26. Tsiku lonse acitira cifundo, nakongoletsa;Ndipo mbumba zace zidalitsidwa.

27. Siyana naco coipa, nucite cokoma,Nukhale nthawi zonse.

28. Pakuti Yehova akonda ciweruzo,Ndipo sataya okondedwa ace:Asungika kosatha:Koma adzadula mbumba za oipa.

29. Olungama adzalandira dziko lapansi,Nadzakhala momwemo kosatha.

30. Pakamwa pa wolungama palankhula zanzeru,Ndi lilime lace linena ciweruzo.

31. Malamulo a Mulungu wace ali mumtima mwace;Pakuyenda pace sadzaterereka.

32. Woipa aunguza wolungama,Nafuna kumupha.

33. Yehova sadzamsiya m'dzanja lace:Ndipo sadzamtsutsa poweruzidwa iye.

34. Yembekeza Yehova, nusunge njira yace,Ndipo Iye adzakukweza kuti ulandire dziko:Pakudutidwa oipa udzapenya,

35. Ndapenya woipa, alikuopsa,Natasa monga mtengo wauwisi wanzika.

36. Koma anapita ndipo taona, kwati zi:Ndipo ndinampwaira osampeza.

37. Tapenya wangwiro, ndipo taona woongoka mtima!Pakuti ku matsiriziro ace a munthuyo kuti mtendere.

38. Koma olakwa adzaonongeka pamodzi:Matsiriziro a oipa adzadutidwa.

39. Koma cipulumutso ca olungama cidzera kwa Yehova,Iye ndiye mphamvu yao m'nyengo ya nsautso.

40. Ndipo Yehova awathandiza, nawalanditsa:Awalanditsa kwa oipa nawapulumutsa,Cifukwa kuti anamkhulupirira Iye,