Masalmo 102 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Wopsinjika apempha Mulungu acitire anthu ace cifundo, amitundu nammverenso

Pemphero la Wozunzika, m'mene anakomoka natsanulira cobnaatira cace pamaso pa Yehova,

1. Yehova, imvani pemphero langa,Ndipo mpfuu wanga ufikire Inu.

2. Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga;Mundichereze khutu lanu;Tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga,

3. Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi,Ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

4. Mtima wanga ukunga udzu wamweta, nufota;Popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5. Cifukwa ca liu la kubuula kwangaMnofu wanga umamatika ku mafupa anga.

6. Ndikunga bvuwo m'cipululu;Ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7. Ndidikira, ndikhala ngati mbawaIri yokha pamwamba pa tsindwi.

8. Adani anga anditonza tsiku lonse;Akundiyarukirawo alumbirira ine.

9. Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,Ndi kusanganiza-comwera canga ndi misozi,

10. Cifukwa ca ukali wanu ndi kuzaza kwanu;Popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11. Masiku anga akunga mthunzi womka m'tali;Ndipo ine ndauma ngati udzu.

12. Koma Inu, Yehova, mukhalabe ku nthawi yonse;Ndi cikumbukilo canu ku mibadwo mibadwo.

13. Inu mudzauka, ndi kucitira nsoni Ziyoni;Popeza yafika nyengo yakumcitira cifundo, nyengo yoikika.

14. Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yace,Nacitira cifundo pfumbi lace.

15. Pamenepo amitundu adzaopa dzina la Yehova,Ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu;

16. Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,Anaoneka m'ulemerero wace;

17. Anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,Osapepula pemphero lao.

18. Ici adzacilembera mbadwo ukudza;Ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19. Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ace opatulika;Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20. Kuti amve kubuula kwa wandende;Namasule ana a imfa,

21. Kuti anthu alalikire dzina la Yehova m'Ziyoni,Ndi cilemekezo cace m'Yerusalemu;

22. Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,Ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23. Iye analanda mphamvu yanga panjira;Anacepsa masiku anga.

24. Ndinati, Mulungu wanga, musandicotse pakati pa masiku anga:Zaka zanu zikhalira m'mibadwo mibadwo.

25. Munakhazika dziko lapansi kalelo;Ndipo zakumwamba ndizo nchito ya manja anu.

26. Zidzatha izi, koma Inu mukhala:Inde, zidzatha zonse ngati cabvala;Mudzazisintha ngati maraya, ndipo zidzasinthika:

27. Koma Inu ndinu yemweyo,Ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28. Ana a atumiki anu adzakhalitsa,Ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.