Masalmo 54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Davide apempha Mulungu amlanditse

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Cilangizo ca Davide. Muja Azift anamuka nauza Sauli, kuti, Kodi Davide sabisala kwathu nanga?

1. Ndipulumutseni, Mulungu, mwa dzina lanu,Ndipo mundiweruze ndi mphamvuyanu.

2. Imvani pemphero langa, Mulungu;Cherani khutu mau a pakamwa panga.

3. Pakuti alendo andiukira,Ndipo oopsa afunafuna moyo wanga;Sadziikira Mulungu pamaso pao.

4. Taonani, Mulungu ndiye mthandizi wanga:Ambuye ndiye wacirikiza moyo wanga.

5. Adzabwezera coipa adani anga:Aduleni m'coonadi canu.

6. Ine mwini ndidzapereka nsembe kwa Inu:Ndidzayamika dzina lanu, Yehova, pakuti nlokoma.

7. Pakuti anandilanditsa m'nsautso yonse;Ndipo ndapenya ndi diso langa ico ndakhumbira pa adani anga,