Masalmo 98 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Alemekeze Mulungu pa cifundo ndi coonadi cao

Sa1mo.

1. Myimbireni Yehova nyimbo yatsopano;Popeza anacita zodabwiza:Dzanja lace lamanja, mkono wace woyera, zinamcitira cipulumutso,

2. Yehova anawadziwitsira cipulumutso cace;Anaonetsera cilungamo cace pamaso pa amitundu.

3. Anakumbukila cifundo cace ndi cikhulupiriko cace ku nyumba ya Israyeli;Malekezero onse a dziko lapansi anaona cipulumutso ca Mulungu wathu.

4. Pfuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi;Kuwitsani ndi kupfuulira mokondwera; inde, yimbirani zomlemekeza.

5. Myimbireni Yehova zomlemekeza ndizeze;Ndi zeze ndi mau a salmo.

6. Pfuulani pamaso pa Mfumu Yehova,Ndi mbetete ndi liu la lipenga,

7. Nyanja Ipfuule ndi kudzala kwace;Dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;

8. Mitsinje iombe manja;Mapiri apfuule pamodzi mokondwera;

9. Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi;Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi cilungamo,Ndi mitundu ya anthu molunjika,