Masalmo 3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Kukhulupirika kwa Mulungu

Salimo la Davide, muja anathawa Abisalomu mwana wace.

1. Yehova! Ha! acuruka nanga akundisautsa ine!Akundiukira ine ndi ambiri.

2. Ambiri amati kwa moyo wanga,Alibe cipulumutso mwa Mulungu.

3. Ndipo Inu Yehova, ndinu cikopa canga;Ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4. Ndipfuula kwa Yehova ndi mau anga,Ndipo andiyankha m'phiri lace loyera,

5. Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo;Ndinauka; pakuti Yehova anandicirikiza.

6. Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7. Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga!Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya;Mwawatyola mano oipawo.

8. Cipulumutso nca Yehova;Dalitso lanu likhale pa anthu anu.