Masalmo 136 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu alemekezedwe pa cifundo cace

1. Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino:Pakuti cifundo cace ncosatha.

2. Yamikani Mulungu wa milungu:Pakuti cifundo cace ncosatha.

3. Yamikani Mbuye wa ambuye:Pakuti cifundo cace ncosatha.

4. Amene yekha acita zodabwiza zazikuru:Pakuti cifundo cace ncosatha.

5. Amene analenga zakumwamba mwanzeru:Pakuti cifundo cace ncosatha.

6. Amene anayala dziko lapansi pamwamba pa madzi:Pakuti cifundo cace ncosatha.

7. Amene analenga miuni yaikuru:Pakuti cifundo cace ncosatha.

8. Dzuwa liweruze usana:Pakuti cifundo cace ncosatha.

9. Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku;Pakuti cifundo cace ncosatha.

10. Iye amene anapandira Aaigupto ana ao oyamba:Pakuti cifundo cace ncosatha.

11. Naturutsa Israyeli pakati pao;Pakuti cifundo cace ncosatha.

12. Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka:Pakuti cifundo cace ncosatha.

13. Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira:Pakuti cifundo cace ncosatha.

14. Napititsa Israyeli pakati pace;Pakuti cifundo cace ncosatha.

15. Nakhutula Farao ndi khamu lace m'Nyanja Yofiira:Pakuti cifundo cace ncosatha.

16. Amene anatsogolera anthu ace m'cipululu:Pakuti cifundo cace ncosatha.

17. Amene anapanda mafumu akulu:Pakuti cifundo cace ncosatha,

18. Ndipo anawapha mafumu omveka:Pakuti cifundo cace ncosatha.

19. Sihoni mfumu ya Aamori;Pakuti cifundo cace ncosatha.

20. Ndi ogi mfumu ya Basana:Pakuti cifundo cace ncosatha.

21. Ndipo anaperekadzikolaolikhale cosiyira;Pakuti cifundo cace ncosatha.

22. Cosiyira ca kwa Israyeli mtumiki wace;Pakuti cifundo cace ncosatha.

23. Amene anatikumbukila popepuka ife;Pakuti cifundo cace ncosatha.

24. Natikwatula kwa otisautsa;Pakuti cifundo cace ncosatha.

25. Ndiye wakupatsa nyama zonse cakudya;Pakuti cifundo cace ncosatha.

26. Yamikani Mulungu wa kumwamba,Pakuti cifundo cace ncosatha.