Masalmo 67 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Amitundu alemekeze Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Neginolo. Salmo, Nyimbo.

1. Aticitire cifundo Mulungu, ndi kutidalitsa,Atiwalitsire nkhope yace;

2. Kuti njira yanu idziwike pa dziko lapansi,Cipulumutso canu mwa amitundu onse.

3. Anthu akuyamikeni, Mulungu;Anthu onse akuyamikeni.

4. Anthu akondwere, napfuule makondwera;Pakuti mudzaweruza anthu malunjika,Ndipo mudzalangiza anthu pa dziko lapansi.

5. Anthu akuyamikeni, Mulungu;Anthu onse akuyamikeni.

6. Dziko lapansi lapereka zipatso zace:Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

7. Mulungu adzatidalitsa;Ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye,