Masalmo 91 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Mulungu asungadi wodzipereka kwa Iye

1. Iye amene akhala pansi m'ngaka yace ya Wam'mwambamwambaAdzagonera mu mthunzi wa Wamphamvuyonse.

2. Ndidzati kwa Yehova, Pothawirapo panga ndi linga langa;Mulungu wanga, amene ndimkhulupirira,

3. Pakuti adzakuonjola ku msampha wa msodzi,Ku mliri wosakaza.

4. Adzakufungatira ndi nthenga zace,Ndipo udzathawira kunsi kwa mapiko ace;Coonadi cace ndico cikopa cocinjiriza.

5. Sudzaopa coopsa ca usiku, Kapena mubvi wopita usana;

6. Kapena mliri woyenda mumdima,Kapena cionongeko cakuthera usana.

7. Pambali pako padzagwa cikwi,Ndi zikwi khumi pa dzanja lamanja lako;Sicidzakuyandikiza iwe.

8. Koma udzapenya ndi maso ako,Nudzaona kubwezera cilango oipa.

9. Popeza udati, Inu Yehova, ndinu pothawirapo pangaUdaika Wam'mwambamwamba cokhalamo cako;

10. Palibe coipa cidzakugwera,Ndipo colanga sicidzayandikiza hema wako.

11. Pakuti adzalamulira angelo ace za iwe,Akusunge m'njira zako zonse.

12. Adzakunyamula pa manja ao,Ungagunde phazi lako pamwala.

13. Udzaponda mkango ndi mphiri;Udzapondereza msona wa mkango ndi cinjoka:

14. Popeza andikondadi ndidzampulumutsa;Ndidzamkweza m'mwamba, papeza adziwa dzina langa.

15. Adzandipfuulira Ine ndipo ndidzamyankha;Kunsautso ndidzakhala naye pamodzi;Ndidzamlanditsa, ndi kumcitira ulemu.

16. Ndidzamkhutitsa ndi masiku ambiri,Ndi kumuonetsera cipulumutso canga,