20. Koma Sihoni sanakhulupirira Israyeli kuti apitire pakati pa malire ace; koma Sihoni anamemeza anthu ace onse, namanga misasa ku Yahazi, nathira nkhondo Israyeli.
21. Ndipo Yehova Mulungu wa Israyeli anapereka Sihoni ndi anthu ace onse m'dzanja la Israyeli, ndipo anawakantha, ndi Israyeli analandira colowa cace, dziko lonse la Aamori, nzika za m'dziko lija.
22. Ndipo analandira akhale colowa cao, malire onse a Aamori, kuyambira Arihoni mpaka Yaboki, ndi kuyambira cipululu mpaka Yordano.
23. Motero Yehova Mulungu wa Israyeli anaingitsa Aamori, pamaso pa anthu ace Israyeli, ndipo kodi liyenera kukhala colowa canu?
24. Cimene akulandiritsani Kemosi mulungu wanu, simucilandira colowa canu kodi? Momwemo ali yense Yehova Mulungu wathu waiogitsa pamaso pathu, zacezo tilandira colowa cathu.
25. Ndipo tsopano kodi inu ndinu wabwino woposa Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Moabu; anatengana konse ndi Israyeli iyeyu kodi, kapena kucita nao nkhondo konse kodi?
26. Pokhala Israyeli m'Hesiboni ndi midzi yace, ndi m'Aroeri ndi midzi yace, ndi m'midzi yonse yokhala m'mphepete mwa Arinoni zaka mazana atatu; munalekeranji kulandanso nthawi ija?
27. Potero sindinakucimwirani ine, koma mundicitira coipa ndinu kundithira nkhondo; Yehova, Woweruzayo, aweruze lero lino pakati pa ana a Israyeli ndi ana a Amoni.
28. Koma mfumu ya ana a Amoni sanamvera mau a Yefita anamtumizirawo.
29. Pamenepo mzimu wa Yehova unamdzera Yefita, napitira iye ku Gileadi, ndi Manase, napitira ku Mizipa wa Gileadi, ndi kucokera ku Mizipa wa Gileadi anapitira kwa ana a Amoni.
30. Ndipo Yefita anawindira Yehova cowinda, nati, Mukaperekatu ana a Amoni m'dzanja langa, ndipo kudzali kuti ciri conse cakuturuka pakhomo pa nyumba yanga kudzakomana nane pakubweranso ine ndi mtendere kucokera kwa ana a Amoni, cidzakhala ca Yehova, ndipo ndidzacipereka nsembe yopsereza.
32. Potero Yefita anapita kwa ana a Amoni kuwathira nkhondo; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja lace;
33. nawakantha kuyambira ku Aroeri mpaka ufika ku Miniti, ndiyo midzi makumi awiri, ndi ku Abelikerami, makanthidwe akuru ndithu. Motero ana a Amoni anagonjetsedwa pamaso pa ana a Israyeli.
34. Pofika Yefita ku Mizipa ku nyumba yace, taonani, mwana wace wamkazi anaturuka kudzakomana naye ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe; ndipo iyeyu anali mwana wace mmodzi yekha, analibe mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.
35. Ndipo kunali, pakumuona anang'amba zobvala zace, nati, Tsoka ine, mwana wanga, wandiweramitsa kwakukuru, ndiwe wa iwo akundisaukitsa ine; pakuti ndamtsegulira Yehova pakamwa panga ine, ndipo sinditha kubwerera.