Oweruza 11:27-38 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Potero sindinakucimwirani ine, koma mundicitira coipa ndinu kundithira nkhondo; Yehova, Woweruzayo, aweruze lero lino pakati pa ana a Israyeli ndi ana a Amoni.

28. Koma mfumu ya ana a Amoni sanamvera mau a Yefita anamtumizirawo.

29. Pamenepo mzimu wa Yehova unamdzera Yefita, napitira iye ku Gileadi, ndi Manase, napitira ku Mizipa wa Gileadi, ndi kucokera ku Mizipa wa Gileadi anapitira kwa ana a Amoni.

30. Ndipo Yefita anawindira Yehova cowinda, nati, Mukaperekatu ana a Amoni m'dzanja langa, ndipo kudzali kuti ciri conse cakuturuka pakhomo pa nyumba yanga kudzakomana nane pakubweranso ine ndi mtendere kucokera kwa ana a Amoni, cidzakhala ca Yehova, ndipo ndidzacipereka nsembe yopsereza.

32. Potero Yefita anapita kwa ana a Amoni kuwathira nkhondo; ndipo Yehova anawapereka m'dzanja lace;

33. nawakantha kuyambira ku Aroeri mpaka ufika ku Miniti, ndiyo midzi makumi awiri, ndi ku Abelikerami, makanthidwe akuru ndithu. Motero ana a Amoni anagonjetsedwa pamaso pa ana a Israyeli.

34. Pofika Yefita ku Mizipa ku nyumba yace, taonani, mwana wace wamkazi anaturuka kudzakomana naye ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe; ndipo iyeyu anali mwana wace mmodzi yekha, analibe mwana wina wamwamuna kapena wamkazi.

35. Ndipo kunali, pakumuona anang'amba zobvala zace, nati, Tsoka ine, mwana wanga, wandiweramitsa kwakukuru, ndiwe wa iwo akundisaukitsa ine; pakuti ndamtsegulira Yehova pakamwa panga ine, ndipo sinditha kubwerera.

36. Ndipo anati kwa iye, Atate wanga, mwamtsegulira Yehova pakamwa panu, mundicitire ine monga umo mudaturutsa mau pakamwa panu; popeza Yehova anakucitirani inu cilango pa adani anu, pa ana a Amoni.

37. Ndipo anati kwa atate wace, Andicitire ici, andileke miyezi iwiri, kuti ndicoke ndi kutsikira kumapiri, ndi kulirira unamwali wanga, ine ndi anzanga.

38. Nati iye, Muka. Namuuza amuke akakhale miyezi iwiri; namuka iye ndi anzace, nalirira unamwali wace pamapiri.

Oweruza 11