Oweruza 11:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yefita Mgileadi ndipo anali ngwazi yamphamvu, ndiye mwana wa mkazi wadama; koma Gileadi adabala Yefita.

2. Ndipo mkazi wa Gileadi anambalira ana amuna; koma atakula ana amuna a mkaziyo anampitikitsa Yefita, nanena naye, Sudzalandira colowa m'nyumba ya atate wako; pakuti ndiwe mwana wa mkazi wina.

3. Pamenepo Yefita anathawa abale ace, nakhala m'dziko la Tobu; ndipo anyamata opanda pace anasonkhana kwa Yefita, naturuka naye pamodzi.

4. Ndipo kunali, atapita masiku, ana a Amoni anacita nkhondo ndi Israyeli,

5. ndipo kunatero, pamene ana a Amoni anathira nkhondo pa Israyeli, akuru a Gileadi anamuka kutenga Yefita m'dziko la Tobu;

6. nati kwa Yefita, Tiye ukhale kazembe wathu kuti tilimbane ndi ana a Amoni.

7. Ndipo Yefita anati kwa akulu a Gileadi, Simunandida kodi, ndi kundicotsa m'nyumba ya atate wanga? ndipo mundidzeraoji tsopano pokhala muli m'kusauka?

8. Ndipo akuru a Gileadi ananena ndi Yefita, Cifukwa cace cakuti takubwerera tsopano ndico kuti umuke nafe ndi kucita nkhondo ndi ana a Amoni, nudzakhala mkuru wathu wa pa onse okhala m'Gileadi.

9. Ndipo Yefita anati kwa akuru a Gileadi, Mukaodifikitsanso kwathu kucita nkhondo ndi ana a Amoni, nakawapereka Yehova pamaso panga, ndidzakhala mkuru wanu kodi?

10. Ndipo akuru a Gileadi anati kwa Yefita, Yehova ndiye wakumvera pakati pa ife, tikapanda kucita monga momwe wanena.

Oweruza 11