Yeremiya 51:42-57 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Nyanja yakwera kufikira ku Babulo; wamira ndi mafunde ace aunyinji.

43. Midzi yace yakhala bwinja, dziko louma, cipululu mosakhalamo anthu, mosapita mwana wa munthu ali yense.

44. Ndipo Ine ndiweruza Beli m'Babulo, ndipo ndidzaturutsa m'kamwa mwace comwe wacimeza; ndipo amitundu sadzasonkhaniranso konse kwa iye; inde, khoma la Babulo lidzagwa.

45. Anthu anga, turukani pakati pace, mudzipulumutse munthu yense ku mkwiyo waukali wa Yehova.

46. Mtima wanu usalefuke, musaope cifukwa ca mbiri imene idzamveka m'dzikomu; pakuti mbiri idzafika caka cina, pambuyo pace caka cina mbiri yina, ndi ciwawa m'dziko, wolamulira kumenyana ndi wolamulira.

47. Cifukwa cace, taonani, masiku alinkudza, amene ndidzaweruza mafano osemasema a Babulo, ndipo dziko lace lonse lidzakhala ndi manyazi; ndipo ophedwa ace onse adzagwa pakati pace.

48. Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi, ndi zonse ziri m'menemo, zidzayimba mokondwerera Babulo; pakuti akufunkha adzafika kwa iye kucokera kumpoto, ati Yehova.

49. Monga Babulo wagwetsa ophedwa a Israyeli, momwemo pa Babulo padzagwa ophedwa a dziko lonse.

50. Inu amene mwapulumuka kulupanga, pitani inu, musaime ciimire; mukumbukire Yehova kutari, Yerusalemu alowe m'mtima mwanu.

51. Tiri ndi manyazi, cifukwa tamva mnyozo; manyazi aphimba nkhope zathu; pakuti alendo alowa m'malo opatulika a nyumba ya Yehova.

52. Cifukwa cace, taona, masiku alinkudza, ati Yehova, amene ndidzaweruza mafano ace; ndipo pa dziko lace lonse olasidwa adzabuula.

53. Ngakhale Babulo adzakwera kumwamba, ngakhale adzalimbitsa msanje wa mphamvu yace, koma kucokera kwa Ine akufunkha adzafika kwa iye, ati Yehova.

54. Mau akupfuula ocokera ku Babulo, ndi a cionongeko cacikuru ku dziko la Akasidi!

55. pakuti Yehova afunkha Babulo, aononga m'menemo mau akuru; ndipo mafunde ace adzakokoma ngati madzi ambiri, mau ao aphokosera;

56. pakuti wakufunkha wafika kwa iye, kwa Babulo, ndi anthu ace olimba agwidwa, mauta ao atyokatyoka, pakuti Yehova ndiye Mulungu wakubwezera, adzabwezera ndithu.

57. Ndipo ndidzaledzeretsa akuru ace ndi anzeru ace, akazembe ace ndi ziwanga zace, ndi anthu ace olimba; ndipo adzagona cigonere, sadzanyamuka, ati Mfumu, dzina lace ndi Yehova wa makamu.

Yeremiya 51