3. Pamenepo Yefita anathawa abale ace, nakhala m'dziko la Tobu; ndipo anyamata opanda pace anasonkhana kwa Yefita, naturuka naye pamodzi.
4. Ndipo kunali, atapita masiku, ana a Amoni anacita nkhondo ndi Israyeli,
5. ndipo kunatero, pamene ana a Amoni anathira nkhondo pa Israyeli, akuru a Gileadi anamuka kutenga Yefita m'dziko la Tobu;
6. nati kwa Yefita, Tiye ukhale kazembe wathu kuti tilimbane ndi ana a Amoni.
7. Ndipo Yefita anati kwa akulu a Gileadi, Simunandida kodi, ndi kundicotsa m'nyumba ya atate wanga? ndipo mundidzeraoji tsopano pokhala muli m'kusauka?
8. Ndipo akuru a Gileadi ananena ndi Yefita, Cifukwa cace cakuti takubwerera tsopano ndico kuti umuke nafe ndi kucita nkhondo ndi ana a Amoni, nudzakhala mkuru wathu wa pa onse okhala m'Gileadi.
9. Ndipo Yefita anati kwa akuru a Gileadi, Mukaodifikitsanso kwathu kucita nkhondo ndi ana a Amoni, nakawapereka Yehova pamaso panga, ndidzakhala mkuru wanu kodi?
10. Ndipo akuru a Gileadi anati kwa Yefita, Yehova ndiye wakumvera pakati pa ife, tikapanda kucita monga momwe wanena.
11. Pamenepo Yefita anamuka ndi akuru a Gileadi, ndipo anthu anamuika mkuru wao ndi mtsogoleri wao; ndipo Yefita ananena mau ace onse pamaso pa Yehova ku Mizipa.
12. Ndipo Yefita anatuma mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni, ndi kuti, Ndi ciani ndi Inu, ndi kuti Mwandidzera kuthira nkhondo dziko langa?
13. Ndipo mfumu ya ana a Amoni inati kwa mithenga ya Yefita, Cifukwa Israyeli analanda dziko langa pakukwera iye kucokera ku Aigupto, kuyambira Arinoni mpaka Yaboki, ndi mpaka Yordano; ndipo tsopano uodibwezere maikowa mwamtendere.
14. Ndipo Yefita anatumanso mithenga kwa mfumu ya ana a Amoni;
15. nanena naye, Atero Yefita, Israyeli sanalanda dziko la Moabu kapena dziko la ana a Amoni;