1 Mbiri 9:10-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndi a ansembe: Yedaya, ndi Yehoyaribu, ndi Yakini,

11. ndi Azariya mwana wa Hilikiya, mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubu, mtsogoleri wa m'nyumba ya Mulungu;

12. ndi Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pasuri, mwana wa Malikiya, ndi Maasai mwana wa Adieli, mwana wa Yazera, mwana wa Mesulamu, mwana wa Mesilemiti, mwana wa Imeri,

13. ndi abale ao, akuru a nyumba za makolo ao cikwi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu ndi limodzi, anthu odziwitsitsa Debito ya utumiki wa nyumba ya Mulungu.

14. Ndi a Alevi: Semaya mwana wal Hasubu, mwana wa Azrikamu, mwana wa Hasabiya, a ana a Merari;

15. ndi Bakabakara, Heresi, ndi Galala, ndi Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zikiri, mwana wa Asafu;

16. ndi Obadiya mwana wa Semaya, mwana wa Galala, mwana wa Yedutuni, ndi Berekiya mwana wa Asa, mwana wa Elikana, wokhala m'midzi ya Anetofati.

17. Ndi odikira pakhomo: Salumu, ndi Akubu, ndi Talimoni, ndi Ahimani ndi abate ao; Salumu ndi mkuru wao,

18. amene adadikira pa cipata ca mfumu kum'mawa mpaka pomwepo, ndiwo odikira pakhomo a tsasa la ana a Levi.

19. Ndipo Salumu mwana wa Kore, mwana wa Ebiasafu; mwana wa Kora, ndi abale ace a nyumba ya atate wace; Akora anayang'anira nchito ya utumiki, osunga zipata za kacisi monga makolo ao; anakhala m'cigono ca Yehova osunga polowera;

20. ndi a Pinehasi mwana wa Eleazara anali mtsogoleri wao kale, ndipo Yehova anali naye.

21. Zekariya mwana wa Meselemiya anali wodikira pakhomo pa cihema cokomanako.

22. Iwo onse osankhidwa akhale odikira kuzipata ndiwo mazana awiri mphambu khumi ndi awiri. Iwo anawerengedwa monga mwa cibadwidwe cao, m'midzi mwao, amene Davide ndi Samueli mlauli anawaika m'udindo wao.

23. Momwemo iwo ndi ana ao anayang'anira zipata za ku nyumba ya Yehova, ndiyo nyumba ya kacisi, m'udikiro wao.

24. Pa mbali zinai panali odikira kum'mawa, kumadzulo, kumpoto, ndi kumwela.

25. Ndi abale ao m'midzi mwao akafikafika, atapita masiku asanu ndi awiri masabata onse, kuti akhale nao;

26. pakuti odikira anai akuru, ndiwo Alevi, anali m'udindo wao, nayang'anira zipinda ndi mosungiramo cuma m'nyumba ya Mulungu.

27. Ndipo amagona usiku m'zipinda zozinga nyumba ya Mulungu, popeza udikiro wace ndi wao; kuitsegula m'mawa ndi m'mawa ndi kwaonso.

1 Mbiri 9