Yesaya 41:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pakuti Ine Yehova Mulungu wako ndidzagwira dzanja lako lamanja, ndi kunena kwa iwe, Usaope ndidzakuthandiza iwe.

14. Usaope, Yakobo, nyongolotsi iwe, ndi anthu inu a Israyeli; ndidzakuthangata iwe, ati Yehova, ndiye Mombolo wako, Woyera wa Israyeli.

15. Taona, ndidzakuyesa iwe coombera tirigu catsopano cakuthwa cokhala ndi mano; iwe udzaomba mapiri ndi kuwapera asalale, ndi kusandutsa zitunda mungu.

16. Iwe udzawakupa, ndi mphepo idzawauluza; ndipo kabvumvulu adzawamwaza; ndipo iwe udzasangalala mwa Yehova, udzadzikuza mwa Woyera wa Israyeli,

17. Wosauka ndi wosowa afuna madzi, ndipo palibe, ndi lilume lao lilephera, cifukwa ca ludzu; Ine Yehova ndidzawayankha, Ine Mulungu wa Israyeli sindidzawasiya.

Yesaya 41