31. Ndipo otsala amene opulumuka a nyumba ya Yuda adzaphukanso mizu pansi, nadzabala cipatso pamwamba.
32. Pakuti mudzaoneka m'Yerusalemu, otsala ndi opulumuka m'Yerusalemu, otsala ndi opulumuka m'phiri la Ziyoni; cangu ca Yehova wa makamu cidzacita ici.
33. Cifukwa cace atero Yehova za mfumu ya Asuri, Iye sadzafika pa mudzi uno, ngakhale kuponyapo mubvi, ngakhale kufika patsogolo pace ndi cikopa, ngakhale kuunjikirapo mulu.
34. Pa njira yomwe anadzerayo, abwerera yomweyo, ndipo sadzafika pa mudzi uno, ati Yehova.
35. Pakuti ndidzacinjiriza mudzi uno, kuupulumutsa, cifukwa ca Ine mwini, ndi mtumiki wanga Davide.
36. Ndipo mthenga wa Yehova anaturuka, naphaipha m'zitando za Asuri, zikwi zana ndi makumi asanu ndi atatu ndi zisanu, ndipo pamene anthu anauka mamawa, taonani, onse ndiwo mitembo.