Yeremiya 6:21-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Cifukwa cace atero Yehova, Taona, ndidzaikira anthuwa zopunthwitsa; ndipo atate ndi ana adzakhumudwa nazo pamodzi; munthu ndi mnzace adzatayika.

22. Yehova atero, Taona, mtundu wa anthu ucokera kumpoto; ndi mtundu waukuru adzaukitsidwa ku malekezero a dziko lapansi.

23. Agwira uta ndi nthungo; ali ankharwe, alibe cifundo; mau ao aphokosera ngati nyanja, akwera pa akavalo; aguba monga anthu ofuna kumenyana nkhondo ndi iwe, mwana wamkazi wa Ziyoni.

24. Tamva ife mbiri yace; manja athu alefuka, yatigwira nkhawa ndi zowawa ngati za mkazi wobala.

25. Usaturukire kumunda, usayenda m'njira; pakuti lupanga la amaliwongo ndi mantha ali m'mbali zonse.

26. Iwe mwana wamkazi wa anthu anga, udzibveke ndi ciguduli, ndi kubvimbvinika m'phulusa; ulire maliro ngati a mwana wamwamuna wa yekha, kulira kowawa koposa; pakuti wakufunkha adzatifikira ife motidzidzimutsa.

Yeremiya 6