Oweruza 21:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma amuna a Israyeli adalumbira ku Mizipa, ndi kuti, Palibe mmodzi wa ife adzapereka mwana wace wamkazi kwa Mbenjamini akhale mkazi wace.

2. Ndipo anthu anadza ku Beteli, nakhala pansi pomwepo pamaso pa Mulungu mpaka madzulo; nakweza mau ao ndi kulira misozi yambiri.

3. Nati iwo, Yehova Mulungu wa Israyeli, cacitika ici cifukwa ninji m'Israyeli kuti lasowa lero pfuko limodzi m'Israyeli?

4. Ndipo kunali m'mawa mwace, anthu analawirira mamawa namangako guwa la nsembe, napereka nsembe zopsereza ndi nsembe zoyamika.

5. Nati ana a Israyeli, Ndani iye mwa mapfuko onse a Israyeli amene sanakwera kudza kumsonkhano kwa Yehova? pakuti panali lumbiro lalikuru pa iye wosakwera kudza kwa Yehova ku Mizipa, ndi kuti, Aphedwe ndithu.

6. Ndipo ana a Israyeli anamva cifundo cifukwa ca Benjamini mbale wao, nati, Pfuko limodzi lalikhidwa pa Israyeli leroli.

Oweruza 21