Oweruza 11:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Yefita Mgileadi ndipo anali ngwazi yamphamvu, ndiye mwana wa mkazi wadama; koma Gileadi adabala Yefita.

2. Ndipo mkazi wa Gileadi anambalira ana amuna; koma atakula ana amuna a mkaziyo anampitikitsa Yefita, nanena naye, Sudzalandira colowa m'nyumba ya atate wako; pakuti ndiwe mwana wa mkazi wina.

3. Pamenepo Yefita anathawa abale ace, nakhala m'dziko la Tobu; ndipo anyamata opanda pace anasonkhana kwa Yefita, naturuka naye pamodzi.

Oweruza 11