Mateyu 8:5-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo m'mene Iye analowa m'Kapernao anadza kwa Iye kenturiyo, nampemba Iye,

6. nati, Ambuye, mnyamata wanga ali gone m'nyumba wodwala manjenje, wozunzidwa koopsa,

7. Ndipo Yesu ananena naye, Ndifika Ine, ndidzamciritsa iye.

8. Koma kenturiyoyo anabvomera nati, Ambuye, sindiyenera kuti mukalowe pansi pa chindwi langa iai; koma mungonena mau, ndipo adzaciritsidwa mnyamata wanga.

9. Pakuti inenso ndiri munthu wakumvera ulamuliro, ndiri nao asilikari akundimvera ine: ndipo ndinena kwa uyu, Muka, namuka; ndi kwa wina, Idza, nadza; ndi kwa kapolo wanga, Cita ici, nacita.

10. Ndipo pakumva ici, Yesu anazizwa, nati kwa iwo akumtsata, Indetu ndinena kwa inu, ngakhale mwa Israyeli, sindinapeza cikhulupiriro cotere.

11. Ndipo ndinena ndi inu, kuti ambiri a kum'mawa ndi a kumadzulo adzafika, nadzakhala pamodzi ndi Abrahamu, ndi Isake, ndi Yakobo, mu Ufumu wa Kumwamba;

12. koma anawo a Ufumu adzatayidwa ku mdima wakunja; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.

13. Ndipo Yesu anati kwa kenturiyoyo, Pita, kukhale kwa iwe monga unakhulupirira. Ndipo anaciritsidwa mnyamatayo nthawi yomweyo.

14. Ndipo pofika Yesu ku nyumba ya Petro, anaona mpongozi wace ali gone, alikudwala malungo.

15. Ndipo anamkhudza dzanja lace, ndipo malungo anamleka mkaziyo; ndipo anauka, namtumikira Iye.

16. Ndipo pakudza madzulo, anabwera nao kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi mizimu yoipa; ndipo Iye anaturutsa mizimuyo ndi mau, naciritsa akudwala onse;

17. kotero kuti cikwaniridwe conenedwa ndi Yesaya mneneri, kuti,Iye yekha anatenga zofoka zathu,Nanyamula nthenda zathu.

18. Ndipo Yesu, poona makamu ambiri a anthu akumzungulira Iye, analamulira ophunzira amuke ku tsidya lina,

19. Ndipo anadza munthu mlembi, nati kwa Iye, Mphunzitsi, ndidzakutsatani Inu kuli konse mumukako.

20. Ndipo Yesu ananena kwa iye, Ankhandwe ali nazo nkhwimba zao, ndi mbalame za m'mlengalenga zisa zao, koma Mwana wa munthu alibe potsamira mutu wace.

21. Ndipo wina wa ophunzira ace anati kwa Iye, Ambuye, mundilole ine nditange ndamuka kuika maliro a atate wanga.

Mateyu 8