Mateyu 23:27-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mufanafana ndi manda opaka njereza, amene aonekera okoma kunja kwace, koma adzala m'katimo ndi mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zonse.

28. Comweco inunso muonekera olungama pamaso pa anthu, koma m'kati muli odzala ndi cinyengo ndi kusayeruzika.

29. Tsoka inu, alembi ndi Afarisi, onyenga! cifukwa mumanga nyumba za pa manda a aneneri, ndipo mukonza manda a anthu olungama,

30. ndi kuti, Ife tikadakhala m'masiku a makolo anthu, sitikadakhala oyanjana nao pa mwazi wa aneneri.

31. Pomwepo mutsimikiza nokha, kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri.

32. Dzazani inu muyeso wa makolo anu.

33. Njoka inu, obadwa inu a mamba, mudzatha bwanji kuthawa kulanga kwace kwa gehena?

34. Cifukwa ca ici, onani, ndituma kwa inu aneneri ndi anzeru ndi alembi; ena a iwo mudzawapha, mudzawapacika; ndi ena a iwo mudzawakwapula m'masunagoge mwanu, ndi kuwazunza, kucokera ku mudzi umodzi, kufikira ku mudzi wina;

35. kotero kuti udzafika pa inu mwazi wonse wotayidwa pa dziko lapansi, kuyambira ku mwazi wa Abele wolungamayo, kufikira ku mwazi wa Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Kacisi ndi guwa la nsembe.

36. Indetu ndinena kwa inu, Zinthu zonse izi zidzafika pa mbadwo uwu wamakono.

37. Ha, Yerusalemu, Yerusalemu, amene umapha aneneri, ndi kuwaponya miyala iwo otumidwa kwa iwe! Ine ndinafuna kangati kusonkhanitsa pamodzi ana ako, inde monga thadzi lisonkhanitsa anapiye ace m'mapiko ace, koma inu simunafuna ai!

38. Onani, nyumba yanu yasiyidwa kwa inu yabwinja.

39. Pakuti ndinena kwa inu, Simudzandionanso Ine, kuyambira tsopano, kufikira mudzanena,Wolemekezedwa Iye amene akudza m'dzina la Ambuye.

Mateyu 23