6. sitinamvera atumiki anu aneneri, amene ananena m'dzina lanu kwa mafumu athu, akalonga athu, makolo athu, ndi anthu onse a m'dziko.
7. Ambuye, cilungamo nca Inu, koma kwa ife manyazi a nkhope yathu, monga lero lino; kwa anthu a Yuda, ndi kwa okhala m'Yerusalemu, ndi kwa Aisrayeli onse okhala pafupi ndi okhala kutali, ku maiko onse kumene mudawaingira, cifukwa ca kulakwa kwao anakulakwirani nako.
8. Ambuye, kwa ife kuli manyazi a nkhope yathu, kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, ndi kwa makolo athu; pakuti takucimwirani.
9. Ambuye Mulungu wathu ndiye wacifundo, ndi wokhululukira; pakuti tampandukira Iye;
10. sitinamvera mau a Yehova Mulungu wathu, kuyenda m'malamulo ace anatiikirawo pamaso pathu, mwa atumiki ace aneneri.
11. Inde Israyeli yense walakwira cilamulo canu, ndi kupambuka, kuti asamvere mau anu; cifukwa cace temberero lathiridwa pa ife, ndi Ilumbiro lolembedwa m'cilamulo ca Mose mtumiki wa Mulungu; pakuti tamcimwira.
12. Ndipo anakwaniritsa mau ace adanenawo, kutitsutsa ife ndi oweruza athu otiweruza, ndi kutitengera coipa cacikuru; pakuti pansi pa thambo lonse sipanacitika monga umo panacitikira Yerusalemu.