Danieli 11:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndi milungu yao yomwe, pamodzi ndi akalonga ao, ndi zipangizo zao zofunika za siliva ndi golidi adzazitenga kumka nazo ndende ku Aigupto; ndi zaka zace zidzaposa za mfumu ya kumpoto.

9. Ndipo adzalowa m'ufumu wa mfumu ya kumwela, koma adzabwera m'dziko lace lace.

10. Ndi ana ace adzacita nkhondo, nadzamemeza makamu a nkhondo akuru ocuruka, amene adzalowa, nadzasefukira, nadzapita; ndipo adzabwerera, nadzacita nkhondo mpaka linga lace.

11. Ndi mfumu ya kumwela adzawawidwa mtima, nadzaturuka kulimbana naye, ndiye mfumu ya kumpoto imene idzaonetsa unyinji waukuru; koma unyinjiwo udzaperekedwa m'dzanja lace.

12. Ndipo ataucotsa unyinjiwo udzakwezeka mtima wace; ndipo adzagwetsa zikwi makumi makumi, koma sadzalakika.

13. Ndi mfumu ya kumpoto idzabwera, nidzaimika unyinji wa kuposa oyamba aja; nidzafika pa cimariziro ca nthawi, ca zaka, ndi khamu lalikuru la nkhondo ndi cuma cambiri.

14. Ndipo nthawi zija ambiri adzaukira mfumu ya kumwela, ndi aciwawa mwa anthu a mtundu wako adzadzikuza kukhazikitsa masomphenyawo, koma adzagwa iwo.

Danieli 11