24. Pomwepo Yoabu anadza kwa mfumu, nati, Mwacitanji? Taonani, Abineri anadza kwa inu, cifukwa ninji tsono munalawirana naye kuti acokedi.
25. Mumdziwa Abineri mwana wa Neri kuti anadza kuti akunyengeni, ndi kuti adziwe kuturuka kwanu ndi kulowa kwanu, ndi kuti adziwe zonse mulikucita inu.
26. Ndipo Yoabu anaturuka kwa Davide, natumizira Abineri mithenga, amene anambweza ku citsime ca Sira. Koma Davide sanacidziwa.
27. Pofikanso Abineri ku Hebroni, Yoabu anampambutsa kupita nave pakati pa cipata kulankhula naye poduka mphepo; namgwaza pomwepo m'mimba, nafa, cifukwa ca mwazi wa Asaheli mbale wace.