1. Ndipo panali nkhondo nthawi yaitali pakati pa nyumba ya Sauli ndi nyumba ya Davide. Koma Davide analimba cilimbire, ndi nyumba ya Sauli inafoka cifokere.
2. Ndipo ana a Davide anabadwira ku Hebroni. Mwana woyamba ndiye Amnoni, wa Ahinoamu wa ku Jezreeli;