15. Yehova wa makamu adzawacinjiriza; ndipo adzadza, nadzapondereza miyala yoponyera; ndipo adzamva, nadzacita phokoso ngati avinyo; ndipo adzadzazidwa ngati mbale, ngati ngondya za guwa la nsembe.
16. Ndipo Yehova Mulungu wao adzawapulumutsa tsiku ilo, ngati zoweta za anthu ace; pakuti adzakhala ngati miyala ya m'korona yakunyezimira pa dziko lace.
17. Pakuti ukoma wace ndi waukuru ndithu, ndi kukongola kwace nkwa kukuru ndithu! tirigu adzakometsera anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.