12. Ndipo anatenga amuna ngati zikwi zisanu, nawaika m'molalira pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa mudzi.
13. Momwemo anaika anthu, khamu lonse lokhala kumpoto kwa mudzi, ndi olalira ao kumadzulo kwa mudzi, ndipo usiku uja Yoswa analowa pakati pa cigwa,
14. Ndipo kunali, pamene mfumu ya ku Ai anaciona, anafulumira iwo, nalawira mamawa, naturuka amuna a m'mudzi kuthirana ndi Israyeli, iye ndi anthu ace onse, poikidwiratu patsogolo pa cidikha; popeza sanadziwa kuti amlalira kukhonde kwa mudzi.
15. Ndipo Yoswa ndi Aisrayeli onse anaoneka ngati a ku Ai alikuwathyola, nathawira njira ya kucipululu.