29. Pamenepo Yoswa ndi Aisrayeli onse naye anapitirira kucokera ku Makeda kumka ku Libina, nathira nkhondo pa Libina;
30. ndipo Yehova anapereka uwunso, ndi mfumu yace m'dzanja la Israyeli; ndipo anaukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi amoyo onse anali m'mwemo, osasiyamo ndi mmodzi yense; namcitira mfumu yace monga anacitira mfumu ya ku Yeriko.
31. Ndipo Yoswa, ndi Aisrayeli onse naye, anapitirira kucokera ku Libina kumka ku Lakisi; namanga misasa, nathira nkhondo pa uwo;
32. napereka Yehova Lakisi m'dzanja la Israyeli, ndipo anaulanda tsiku laciwiri, naukantha ndi lupanga lakuthwa, ndi amoyo onse anali m'mwemo monga mwa zonse anacitira Libina.