2. Ndipo munthu adzakhala monga pobisalira mphepo, ndi pousira cimphepo; monga mitsinje yamadzi m'malo ouma, monga mthunzi wa thanthwe lalikuru m'dziko lotopetsa.
3. Ndipo maso a iwo amene aona sadzatsinzina, ndi makutu a iwo amene amva adzamvera.
4. Mtimanso wansontho udzadziwa nzeru, ndi lilume la acibwibwi lidzalankhula zomveka msanga.
5. Wopusa sadzayesedwanso woolowa manja, ngakhale wouma manja sadzayesedwa mfulu.
6. Pakuti wopusa adzanena zopusa, ndi mtima wace udzacita mphulupulu, kucita zoipitsa, ndi kunena za Yehova molakwira, kusowetsa konse mtima wanjala, ndi kulepheretsa cakumwa ca waludzu.