Yesaya 13:4-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Mau a khamu m'mapiri, akunga amtundu waukuru wa anthu, mau a phokoso la maufumu a mitundu yosonkhanidwa! Yehova wa makamu asonkhanitsa khamu kunkhondo.

5. Acokera m'dziko lakutari, ku malekezero a thambo, ngakhale Yehova, ndi zida za mkwiyo wace, kuti aononge dziko lonse.

6. Kuwani inu; pakuti tsiku la Yehova liri pafupi; lidzafika monga cionongeko cocokera kwa Wamphamvuyonse.

7. Cifukwa cace manja onse adzafoka, ndi mitima yonse ya anthu idzasungunuka;

8. ndipo adzaopa; zowawa ndi masauko zidzawagwira; ndipo adzamva zowawa, ngati mkazi wakubala; adzazizwa wina ndi wina; nkhope zao zidzanga malawi a moto.

Yesaya 13