Yeremiya 51:43-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Midzi yace yakhala bwinja, dziko louma, cipululu mosakhalamo anthu, mosapita mwana wa munthu ali yense.

44. Ndipo Ine ndiweruza Beli m'Babulo, ndipo ndidzaturutsa m'kamwa mwace comwe wacimeza; ndipo amitundu sadzasonkhaniranso konse kwa iye; inde, khoma la Babulo lidzagwa.

45. Anthu anga, turukani pakati pace, mudzipulumutse munthu yense ku mkwiyo waukali wa Yehova.

46. Mtima wanu usalefuke, musaope cifukwa ca mbiri imene idzamveka m'dzikomu; pakuti mbiri idzafika caka cina, pambuyo pace caka cina mbiri yina, ndi ciwawa m'dziko, wolamulira kumenyana ndi wolamulira.

47. Cifukwa cace, taonani, masiku alinkudza, amene ndidzaweruza mafano osemasema a Babulo, ndipo dziko lace lonse lidzakhala ndi manyazi; ndipo ophedwa ace onse adzagwa pakati pace.

48. Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi, ndi zonse ziri m'menemo, zidzayimba mokondwerera Babulo; pakuti akufunkha adzafika kwa iye kucokera kumpoto, ati Yehova.

49. Monga Babulo wagwetsa ophedwa a Israyeli, momwemo pa Babulo padzagwa ophedwa a dziko lonse.

50. Inu amene mwapulumuka kulupanga, pitani inu, musaime ciimire; mukumbukire Yehova kutari, Yerusalemu alowe m'mtima mwanu.

Yeremiya 51