Yeremiya 51:31-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. Wamtokoma mmodzi adzathamanga kukakomana ndi mnzace, ndi mthenga mmodzi kukomana ndi mnzace, kukauza mfumu ya ku Babulo kuti mudzi wace wagwidwa ponsepo;

32. pamadooko patsekedwa, pamatamanda a mabango patenthedwa ndi moto, ndi anthu a nkhondo aopa.

33. Pakuti atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Mwana wamkazi wa Babulo akunga dwale pamene aliunda; patsala kanthawi kakang'ono, ndipo nthawi yamasika idzamfikira iye.

34. Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo wandidya ine, wandiphwanya ine, wandiyesa ine ngati mbiya yopanda kanthu, wandimeza ngati ng'ona, wadzaza m'kamwa mwace ndi zotsekemera zanga, wanditaya ine,

Yeremiya 51