Numeri 3:27-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Banja la Aamiramu, ndi banja la Aizara, ndi banja la Ahebroni, ndi banja la Auziyeli ndiwo a Kohati; ndiwo mabanja a Akohati.

28. Powawerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu ndiwo zikwi zisanu ndi zitatu mphambu mazana asanu ndi limodzi, akusunga udikiro wa pa malo opatulika.

29. Mabanja a ana a Kohati azimanga mahema ao pa mbali ya kacisi ya kumwera.

30. Ndipo kalonga wa nyumba ya makolo ao ya mabanja a Akohati ndiye Elizafana mwana wa Uziyeli.

31. Ndipoudikirowaondiwo likasa, ndi gome, ndi coikapo nyali, ndimagome a nsembe, ndi zipangizo za malo opatulika zimene acita nazo, ndi nsaru yocinga, ndi nchito zace zonse.

32. Ndipo kalonga wa akalonga a Alevi ndiye Eleazara mwana wa Aroni wansembeyo; ndiye aziyang'anira osunga udikiro wa pa malo opatulika.

33. Banja la Amali, ndi banja la Amusi ndiwo a Merari; ndiwo mabanja a Merari.

34. Ndipo owerengedwa ao, powerenga amuna onse, kuyambira a mwezi umodzi ndi mphambu, ndiwo zikwi zisanu ndi cimodzi kudza mazana awiri.

35. Ndi kalonga wa nyumba ya makolo ya mabanja a Merari ndiye Zuriyeli mwana wa Abiyaili; azimanga mahema ao pa mbali ya kacisi ya kumpoto.

36. Ndipo coyang'anira iwo, udikiro wao wa ana a Merari ndiwo matabwa a kacisi, ndi mitanda yace, ndi mizati ndi nsanamira zace, ndi makamwa ace, ndi zipangizo zace zonse, ndi nchito zace zonse;

37. ndi nsici za pabwalo pozungulira, ndi makamwa ace, ndi ziciri zace, ndi zingwe zace.

Numeri 3