Mlaliki 11:6-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Mamawa fesa mbeu zako, madzulonso osapumitsa dzanja lako; pakuti sudziwa ziti zidzalola bwino ngakhale izizi, ngakhale izozo, kaya zonse ziwiri zidzakhala bwino.

7. Indetu kuunika nkokoma, maso napeza bwino m'kuona dzuwa.

8. Inde, munthu akakhala ndi moyo zaka zambiri, akondwere ndi zonsezo; koma akumbukire masiku amdima kuti adzacuruka. Zonse zirinkudza ziri zacabe.

Mlaliki 11