Miyambi 4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Ceniezo lakuti afune Nzeru nalewe njira za oipa

1. Ananu, mverani mwambo wa atate,Nimuchere makutu mukadziwe luntha;

2. Pakuti ndikuphunzitsani zabwino;Musasiye cilangizo canga.

3. Pakuti ndinali mwana kwa atate wanga,Wokondedwa ndi mai, ndine ndekha, sanabala wina.

4. Atate nandiphunzitsa, nati kwa ine,Mtima wako uumirire mau anga;Sunga malamulo anga, nukhale ndi moyo.

5. Tenga nzeru, tenga luntha;Usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;

6. Usasiye nzeru, ndipo Idzakusunga;Uikonde, idzakucinjiriza.

7. Nzeru ipambana, tatenga nzeru;M'kutenga kwako konseko utenge luntha.

8. Uilemekeze, ndipo idzakukweza;Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.

9. Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako;Idzakupatsa korona wokongola.

10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.

11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.

12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.

13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.

14. Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.

15. Pewapo, osapitamo;Patukapo, nupitirire.

16. Pakuti akapanda kucita zoipa, samagona;Ndipo akapanda kukhumudwitsa wina, tulo tao tiwacokera.

17. Pakuti amadya cakudya ca ucimo,Namwa vinyo wa cifwamba.

18. Koma mayendedwe a olungama akunga kuunika kwa mbanda kuca,Kunkabe kuwala kufikira usana woti mbe.

19. Njira ya oipa ikunga mdima;Sadziwa cimene ciwapunthwitsa,

20. Mwananga, tamvera mau anga;Cherera makutu ku zonena zanga.

21. Asacoke ku maso ako;Uwasunge m'kati mwa mtima wako.

22. Pakuti ali moyo kwa omwe awapeza,Nalamitsa thupi lao lonse.

23. Cinjiriza mtima wako koposa zonse uzisunga;Pakuti magwero a moyo aturukamo.

24. Tasiya m'kamwa mokhota,Uike patari milomo yopotoka.

25. Maso ako ayang'ane m'tsogolo,Zikope zako zipenye moongoka,

26. Sinkasinkha bwino mayendedwe a mapazi ako;Njira zako zonse zikonzeke.

27. Usapatuke ku dzanja lamanja kapena kulamanzere;Suntha phazi lako kusiya zoipa.