Miyambi 10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Miyambo yosiyana-siyana; Miyambo ya Sotomo

1. Mwana wanzeru akondweretsa atate;Koma mwana wopusa amvetsa amace cisoni.

2. Cuma ca ucimo sicithangata:Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.

3. Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;Koma amainga cifuniro ca wocimwa.

4. Wocita ndi dzanja laulesi amasauka;Koma dzanja la akhama lilemeretsa.

5. Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru;Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.

6. Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

7. Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.

8. Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.

9. Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.

10. Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.

11. M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.

12. Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.

13. Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.

14. Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.

15. Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;Koma umphawi wao uononga osauka.

16. Nchito za wolungama zipatsa moyo;Koma phindu la oipa licimwitsa.

17. Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo;Koma wosiya cidzudzulo asocera.

18. Wobisa udani ali ndi milomo yonama;Wonena ugogodi ndiye citsiru.

19. Pocuruka mau zolakwa sizisoweka;Koma wokhala cete acita mwanzeru.

20. Lilime la wolungama likunga siliva wosankhika;Koma mtima wa oipa uli wacabe.

21. Milomo ya wolungama imadyetsa ambiri;Koma zitsiru zimafa posowa nzeru.

22. Madalitso a Yehova alemeretsa,Saonjezerapo cisoni.

23. Masewero a citsiru ndiwo kucita zoipa;Koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.

24. Comwe woipa aciopa cidzamfikira;Koma comwe olungama acifuna cidzapatsidwa.

25. Monga kabvumvulu angopita, momwemo woipa kuti zi;Koma olungama ndiwo maziko osatha.

26. Ngati vinyo wowawa m'mano, ndi utsi m'maso,Momwemo wolesi kwa iwo amene amtuma.

27. Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;Koma zaka za oipa zidzafinimpha,

28. Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe;Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.

29. Njira ya Yehova ndi linga kwa woongoka mtima;Koma akucita zoipa adzaonongeka.

30. Wolungama sadzacotsedwa konse:Koma oipa sadzakhalabe m'dziko.

31. M'kamwa mwa wolungama mulankhula nzeru;Koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32. Milomo ya wolungama idziwa zokondweretsa;Koma m'kamwa mwa oipa munena zokhota,