Mateyu 9:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Iye analowa m'ngalawa, naoloka, nadza kumudzi kwao.

2. Ndipo onani, anabwera naye kwa Iye munthu wamanjenje, wakugona pachika: ndipo Yesu pakuona cikhulupiriro cao, anati kwa wodwalayo, Limba mtima, mwana, macimo ako akhululukidwa.

3. Ndipo onani, ena a alembi ananena mumtima mwao, Uyu acitira Mulungu mwano.

4. Ndipo Yesu, pozindikira maganizo ao, anati, Cifukwa canji mulinkuganizira zoipam'mitimayanu?

5. pakuti capafupi nciti, kunena, Macimo ako akhululukidwa; kapena kunena, Tanyamuka nuyende?

6. Koma kuti mudziwe kuti ali nazo mphamvu Mwana wa munthu pansi pano za kukhululukira macimo (pomwepo ananena kwa wodwalayo), Tanyamuka, nutenge chika lako, numuke kunyumba kwako.

Mateyu 9