Mateyu 13:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. ndipo popeza zinalibe mizu zinafota.

7. Koma zina zinagwa paminga, ndipo mingayo inayanga, nizitsamwitsa izo.

8. Koma zina zinagwa pa nthaka yabwino, ndipo zinabala zipatso, zina za makumi khumi, zina za makumi asanu ndi limodzi, zina za makumi atatu.

9. Amene ali ndi makutu, amve.

10. Ndipo ophunzirawo anadza, nati kwa Iye, Cifukwa canji muphiphiritsira iwo m'mafanizo?

11. Ndipo Iye anayankha nati, Cifukwa kwapatsidwa kwa inu kudziwa zinsinsi za Ufumu wa Kumwamba, koma sikunapatsidwa kwa iwo.

12. Pakuti yense amene ali nazo, kudzapatsidwa kwa iye, ndimo adzakhala nazo zocuruka; koma yense amene alibe, cingakhale comwe ali naco cidzacotsedwa kwa iye.

13. Cifukwa cace ndiphiphiritsira iwo m'mafanizo; cifukwa kuti akuona samaona, ndi akumva samamva, kapena samadziwitsa.

14. Ndipo adzacitidwa kwa iwo mau adanenera Yesaya, amene ati.Pakumva mudzamva, ndipo simudzazindikira konse;Pakupenya mudzapenya, ndipo simudzaona konse;

15. Cifukwa unalemera mtima wa anthuawa,Ndipo m'makutu ao anamva mogontha,Ndipo maso ao anatsinzina;Kuti asaone konse ndi maso,Asamve ndi makutu,Asazindikire ndi mtima wao,Asatembenuke,Ndipo ndisawaciritse iwo.

16. Koma maso anu ali odala, cifukwa apenya; ndi makutu anu cifukwa amva.

17. Pakuti indetu ndinena kwa inu, kuti aneneri ambiri ndi anthu olungama analakalaka kupenya zimene muziona, koma sanaziona; ndi kumva zimene muzimva, koma sanazimva.

18. Ndipo tsono mverani inu fanizolo la wofesa mbeu uja.

19. Munthu ali yense wakumva mau a Ufumu, osawadziwitsai, woipayo angodza, nakwatula cofesedwaco mumtima mwace. Uyo ndiye wofesedwa m'mbali mwa njira.

20. Koma iye amene afesedwa pamiyala, uyu ndiye wakumva mau, ndi kuwalandira pomwepo ndi kusekera;

Mateyu 13