47. Ndiponso, Ufumu wa Kumwamba uli wofanana ndi khoka loponyedwa m'nyanja, ndi 1 kusonkhanitsa pamodzi za mitundu yonse;
48. limene podzala, analibvuulira pamtunda; ndipo m'mene anakhala pansi, anazisonkhanitsa zabwino m'zotengera, koma zoipa anazitaya kuthengo.
49. Padzatero pa cimariziro ca nthawi ya pansi pano: angelo adzaturuka, 2 nadzawasankhula oipa pakati pa abwino,
50. nadzawataya m'ng'anjo yamoto; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.
51. Mwamvetsa zonsezi kodi? lwo anati kwa Iye, inde.
52. Ndipo Iye anati kwa iwo, Cifukwa cace, mlembi ali yense, wophunzitsidwa mu Ufumu wa Kumwamba, ali wofanana ndi munthu mwini banja, amene aturutsa m'cuma cace zinthu zakale ndi zatsopano.
53. Ndipo panali, pamene Yesu anatha mafanizo awa, anacokera kumeneko.
54. Ndipo 3 pofika ku dziko la kwao, anaphunzitsa iwo m'sunagoge mwao, kotero kuti anazizwa, nanena, Uyu adazitengakuti nzeru zimenezi ndi zamphamvu izi?
55. 4 Kodi uyu si mwana wa mmisiri wa mitengo? kodi dzina lace la amace si Mariya? ndi 5 abale ace si Yakobo ndi Yosefe ndi Simoni ndi Yuda?
56. Ndipo alongo ace sali ndife onsewa? Ndipo iyeyo adazitenga zinthu zonsezi kuti?
57. Ndipo iwo anakhumudwa cifukwa ca Iye. Koma Yesu anati kwa iwo, 6 Mneneri sakhala wopanda ulemu koma ku dziko la kwao ndiko, ndi kubanja kwace.
58. Ndipo Iye, cifukwa ca kusakhulupirira kwao, sanacita kumeneko zamphamvu zambiri.