Mateyu 10:1-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo pamene Iye anadziitanira ophunzira ace khumi ndi awiri, anapatsa iwo mphamvu pa mizimu yoipa, yakuiturutsa, ndi yakuciza nthenda iri yonse ndi zofoka zonse.

2. Ndipo maina ao a atumwiwo khumi ndi awiri ndi awa: woyamba Simoni wochedwa Petro, ndi Andreya mbale wace; Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi Yohane mbale wace;

3. Filipo, ndi Bartolomeyo; Tomasi, ndi Mateyu wamsonkhoyo; Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Tadeyo;

4. Simoni Mkanani, ndi Yudasi Isikariote amenenso anampereka Iye.

5. Awa amene, khumi ndi awiriwa, Yesu anawatumiza, nawalangiza ndi kuti,Musapite ku njira ya kwa anthu akunja, ndi m'mudzi wa Asamariya musamalowamo:

6. koma makamaka mupite ku nkhosa zosokera za banja la Israyeli.

7. Ndipo pamene mulikupita lalikani kuti, Ufumu wa Kumwamba wayandikira.

8. Ciritsani akudwala, ukitsani akufa, konzani akhate, turutsani ziwanda: munalandira kwaulere, patsani kwaulere.

9. Musadzitengere ndalama zagolidi, kapena zasiliva, kapena zakobiri m'malamba mwanu;

10. kapena thumba la kamba la kunjira, kapena malaya awiri, kapena nsapato, kapena ndodo; pakuti wanchito ayenera kulandira zakudya zace.

11. Ndipo m'mzinda uliwonse, kapena m'mudzi mukalowamo, mufunsitse amene ali woyenera momwemo; ndipo bakhalani komweko kufikira muturukamo.

Mateyu 10