Ezekieli 48:27-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndi ku malire a Zebuloni, kuyambira ku mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; Gadi, limodzi.

28. Ndi ku malire a Gadi, mbali ya kumwela, kuloza kumwela, malire akhale kuyambira ku Tamara kufikira ku madzi a Meribati ndi Kadesi, ku mtsinje wa Aigupto, kufikira ku nyanja yaikuru.

29. Ili ndi dziko muligawire mafuko a Israyeli ndi kucita maere, likhale colowa cao; ndipo awa ndi magawo ao, ati Ambuye Yehova.

30. Ndipo malekezero a mudzi ndi awa: mbali ya kumpoto avese mabango zikwi zinai mphambu mazana asanu;

31. ndi zipata za mudzi zidzakhala monga mwa maina a mafuko a Israyeli; zipata zitatu kumpoto: cipata cimodzi ca Rubeni, cipata cimodzi ca Yuda, cipata cimodzi ca Levi;

32. ndi ku mbali ya kum'mawa zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zitatu: cipata cimodzi ca Yosefe, cipata cimodzi ca Benjamini, cipata cimodzi ca Dani;

33. ndi ku mbali ya kumwela ayese zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zitatu: cipata cimodzi ca Simeoni, cipata cimodzi ca Isakara, cipata cimodzi ca Zebuloni;

34. ku mbali ya kumadzulo zikwi zinai mphambu mazana asanu, ndi zipata zace zitaru; cipata cimodzi ca Gadi, cipata cimodzi ca Aseri, cipata cimodzi ca Nafitali.

Ezekieli 48