Ezekieli 39:24-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndinacita nao monga mwa kudetsedwa kwao, ndi monga mwa kulakwa kwao, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.

25. Cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Tsopano ndidzabweza undende wa Yakobo, ndi kucitira cifundo nyumba yonse ya Israyeli, ndipo ndidzacitira dzina langa loyera nsanje.

26. Ndipo adzasenza manyazi ao, ndi zolakwa zao zonse, zimene anandilakwira nazo, pokhala mosatekeseka iwo m'dziko lao, opanda wina wakuwaopsa;

27. nditabwera nao kucoka kwa mitundu ya anthu, nditawasokolotsa m'maiko a adani ao, ndi kuzindikiridwa Woyera mwa iwo pamaso pa amitundu ambiri.

Ezekieli 39