Danieli 8:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka cacitatu ca Belisazara mfumu masomphenya anandionekera kwa ine Danieli, atatha kundionekera oyamba aja.

2. Ndipo ndinaona m'masomphenya; tsono kunali, pakuwaona ine ndinali m'Susani, m'nyumba ya mfumu, ndiwo m'dziko la Elamu; ndinaona m'masomphenya kuti ndinali kumtsinje Ulai.

3. Ndipo ndinakweza maso anga ndi kupenya; taonani, panaima pamtsinje nkhosa yamphongo yokhala nazo nyanga ziwiri, ndi nyanga ziwirizo zinali za msinkhu wautali, koma imodzi inaposa inzace; yoposayo inaphuka m'mbuyo.

4. Ndinaona nkhosa yamphongo irikugunda kumadzulo, ndi kumpoto, ndi kumwela; ndipo panalibe zamoyo zokhoza kuima pamaso pace; panalibenso wakulanditsa m'dzanja lace; koma inacita monga mwa cifuniro cace, nidzikulitsa.

5. Ndipo polingirfrapo ine, taonani, wadza tonde wocokera kumadzulo, pa nkhope ya dziko lonse lapansi, wosakhudza nthaka; ndi mbuziyo inali ndi nyanga yooneka bwino pakati pa maso ace.

6. Ndipo anadzera nkhosa yamphongoyo yokhala ndi nyanga ziwiri, imene ndidaiona irikuima kumtsinje, naithamangira ndi mphamvu yace yaukali.

Danieli 8