Danieli 3:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pamenepo Nebukadinezara, mumkwiyo ndi m'ukali wace, anawauza abwere nao Sadrake, Mesake, ndi Abedinego. Ndipo anabwera nao amunawa kwa mfumu.

14. Nebukadinezara anayankha, nati kwa iwo, Kodi mutero dala, Sadrake, Mesake, ndi Abedinego, kusatumikira milungu yanga, ndi kusalambira fano lagolidi ndinaliimikalo?

15. Mukabvomereza tsono, pakumva mau a lipenga, citoliro, zeze, sansi, cisakasa, ndi ngoli, ndi zoyimbitsa ziri zonse, kugwadira ndi kulambira fano ndinalipanga, cabwino; koma mukapanda kulambira, mudzaponyedwa nthawi yomweyi m'kati mwa ng'anjo yotentha yamoto; ndipo mulungu amene adzakulanditsani m'manja mwanga ndani?

16. Sadrake, Mesake, ndi Abedinego, anayankha, nati kwa mfumu Nebukadinezara, Sikufunika kuti tikuyankheni pa mlandu uwu.

17. Taonani, Mulungu wathu amene timtumikira akhoza kutilanditsa m'ng'anjo yotentha yamoto, nadzatilanditsa m'dzanja lanu, mfumu.

Danieli 3