Cibvumbulutso 12:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo cizindikilo cacikuru cinaoneka m'mwamba; mkazi wobvekedwa dzuwa, ndi mwezi ku mapazi ace, ndi pamutu pace korona wa nyenyezi khumi ndi ziwiri;

2. ndipo anali ndi pakati; ndipo apfuula alimkubala, ndi kumva zowawa zakubala.

3. Ndipo cinaoneka cizindikilo cina m'mwamba, taonani, cinjoka cofiira, cacikuru, cakukhala nayo mitu isanu ndi iwiri, ndi nyanga khumi, ndi pamutu pace nduwira zacifumu zisanu ndi ziwiri.

Cibvumbulutso 12