12. Ndipo Davide anazindikira kuti Yehova anamkhazikitsa mfumu ya Israyeli, ndi kuti anakulitsa ufumu wace cifukwa ca anthu ace Israyeli.
13. Ndipo Davide anadzitengera akazi ang'ono ena ndi akazi a ulemu ena a ku Yerusalemu, atafikako kucokera ku Hebroni; ndipo anambadwira Davide ana amuna ndi akazi.
14. Maina a iwo anambadwira m'Yerusalemu ndi awa: Samua, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomo,
15. ndi Ibara ndi Elisua, ndi Nefegi ndi Yafiya;
16. ndi Elisama ndi Eliada ndi Elifeleti.
17. Koma pamene Afilisti anamva kuti adamdzoza Davide mfumu ya Israyeli, Afilisti onse anakwera kukafuna Davide; ndipo Davide anacimva natsikira kungaka kuja.
18. Tsono Afilisti anafika natanda m'cigwa ca Refaimu.