2 Samueli 3:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. ndi wacinai Adoniya mwana wa Hagiti; ndi wacisanu Sefatiya mwana wa Abitali;

5. ndi wacisanu ndi cimodzi Itireamu wa Egila mkazi wa Davide. Awa anambadwira Davide ku Hebroni.

6. Ndipo panali, pokhala nkhondo pakati pa nyumba ya Sauli ndi nyumba ya Davide, Abineri analimbikira nyumba ya Sauli.

7. Ndipo Sauli adali ndi mkazi wamng'ono, dzina lace ndiye Rizipa, mwana wa Aya. Ndipo Isiboseti anati kwa Abineri, Unalowana bwanji ndi mkazi wamng'ono wa atate wanga?

2 Samueli 3