15. Ndipo anadza nammangira misasa m'Abeli wa Betimaaka, naundira nthumbira pa mudziwo, ndipo unagunda tioga; ndipo anthu onse akukhala ndi Yoabu anakumba lingalo kuti aligwetse.
16. Pamenepo mkazi wanzeru wa m'mudzimo anapfuula, kuti, Imvani, imvani; munene kwa Yoabu, Bwerani pafupi kuno kuti ndgankhule nanu.
17. Ndipo anayandikira kwa mkaziyo; ndi mkaziyo anati, Ndinu Yoabu kodi? iye nayankha, Ndine amene. Pamenepo ananena naye, Imvani mau a mdzakazi wanu. Iye nayankha, Ndirikumva.
18. Ndipo iye analankhula, nati, Kale adafunena kuti, Zoonadi adzapempha uphungu ku Abeli; ndipo potero mrandu udafukutha.
19. Inendine wa awo amene ali amtendere ndi okhulupirika m'Israyeli; inu mulikufuna kuononga mudzi ndi mai wa m'Israyeli; mudzamezerang colowa ca Yehova?
20. Ndipo Yoabu anayankha nati, Iai ndi pang'ono ponse, cikhale kutali kwa ine, kuti ndingameze ndi kuononga.